Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 63

Miyambi ya Patsokwe kuyankhula chimene akufuna. Vuto limakhalapo ngati atachita zinthu zophwanya malamulo. Gulo akasowa mtengo, amazungulira chitsa. -Pamlandu munthu ayenera kugwiritsa ntchito umboni uli- wonse umene uli nawo. Chimodzimodzinso pamoyo wathu, ngati tasowa chinthu tiyenera kupeza china choti chilowe m’malo mwake. Gumula zikulake. -N’zosavuta kupeza zolakwa za wina, kuwononga zinthu, ko- manso kugwiritsa ntchito zomwe wina wapanga. Koma kuti upange zako pamakhala matatalazi. Gunda umvetse. -Pofuna kudziwa zoona zenizeni, munthu umayenera kufunsa kapena kuchita zinthuzo. Gunya sasenda, amene wasenda wakhuta. -Mukamadya mbatata, anthu anjala sasenda, akayamba kusenda ndiye kuti ayamba kukhuta. Choncho, tikamagwira ntchito, zomwe tingathe kusiya osazigwiritsa ntchito tisataye nazo nthawi. Gwada utame, ndikuuze chinapha mako. -Mawuwa amanenedwa munthu akamalimbikitsa mnzake kuti asabise chomwe wabwerera, kuti akatero nayenso amuuze zin- thu zina zachinsisi. Gwada, umvetse. -Pofuna kumvetsa kanthu kenake pafunika kudekha, kudzi- chepetsa ndi kupempha kuti wina akuthandize. Gwadugwadu ndiko chikulu, chilili ndiko kupusa. -Kugwada pamene munthu wamkulu akuyankhula ndi ulemu 62