Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 62

Miyambi ya Patsokwe zabwino nthawi zonse. Nthawi zina munthu amakumana ndi mavuto. Golo! kumtondo, kumunda kulibe ndime. -Mawuwa amanena za munthu waulesi, yemwe amakonda kudya koma n’kumakana kugwira ntchito. Gomo likagumuka, zako umadyeratu. -Pamavuto munthu amayenera kuchita chilichonse kuti adzipu- lumutse. Gona n’kuphe sali kutali. -Mawa si kalekale, ngati mmene zimakhalira ndi munthu amene wauzidwa kuti aphedwa mawa. Nthawi imadutsa mofulumira kwambiri. Gona n’kuphe sikutali. -Mawa si kalekale, ngati mmene zimakhalira ndi munthu amene wauzidwa kuti aphedwa mawa. Nthawi imadutsa mofulumira kwambiri. Gonu, kwacha; masiku adyana. -Munthu aliyense ayenera kukhala wokonzekera kugwira ntchi- to chifukwa zamawa sizidziwika. Gule aliyense amakoma potsiriza. -Chinthu chilichonse chimakhala chovuta komanso chosasan- galalatsa ukamachiyamba. Koma ukachizolowera chimayamba kukusangalatsa. Gule n’guleje, umakumbuka podya nkhwani. -Osamakomedwa ndi zosangalatsa za m’dzikoli n’kufika poiwa- la Mulungu kapena kuiwala zoti ukhoza kukumana ndi mavuto kapena kufa kumene. Gule ndi wa aliyense, kulakwa n’kuthyola mwendo. -Munthu aliyense ali ndi ufulu wokhala, kuchita komanso 61