Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 61

Miyambi ya Patsokwe ngati mmene amachitira Galu amene anasochera ndi goli lake. Galu wakuba amaipitsa mbiri ya ana ake. -Zimene munthu m’modzi angachite zikhoza kuipitsa mbiri ya mtundu wake wonse kapena banja lake. Galu wamiliri anaba nyama n’kuoloka nayo mtsinje. -Munthu wopirira ndi amene amapindura nthawi zambiri. Kha- ma limathandiza kuti munthu apeze chomwe akufuna. Galu wamiliri anaoloka mtsinje. -Munthu wopirira ndi amene amapindura nthawi zambiri. Kha- ma limathandiza kuti munthu apeze chomwe akufuna. Galu wamkota sakandira pachabe. -Akuluakulu akamatichenjeza ndiye kuti alinga ataona kuopsa kwa zimene tikuchitazo. Choncho, ndi bwino kumawamvera kuti tipewe mavuto. Mwachitsanzo, galu wamkota, san- gangokanda popanda kanthu. Mutafufuza mukhoza kupeza kuti pali nyama. Galu wandifera m’khwapa. -Mawuwa amaneneda potanthauza kuti zangovuta koma tinaye- setsa. Galu wofewerera anapita ndi khongozi (goli). -Munthu akakhala wotengeka ndi zonena za ena komanso madandaulo a ena amasochera. Galu wouwa saluma. -Munthu woyankhulayankhula nthawi zambiri amakhala wopanda mnzeru kapena wopanda mphamvu. Gola akasowa Nkhuku, amatola udzu. -Gola kapena kuti mphamba, imakonda kugwira Nkhuku. Ko- ma zikavuta, imatha kudya udzu. Tisamangoyembekeza 60