Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 60

Miyambi ya Patsokwe Galu adaipitsa yekha alendo. -Mwambiwu umanena za munthu amene wadziwonongera tsogolo pochita zinthu zosayenera. Galu akati phethi, wataya nyama. -Pogwira ntchito kapena pochita chinthu chilichonse, monga maphunziro, sipamafunika kuyang’ana m’mbuyo kapena kugwa mphwayi koma kudzipereka ndi mtima wonse. Ukapusa umapezeka kuti wataya mwayi. Galu ndi galu basi. -Munthu amene ali ndi khalidwe kapena chizolowezi chinachake zimavuta kuti asinthe. Galu sasowa mbuyake. -N’zofunika kuti nthawi zonse tizikumbukira amene amatithan- diza, monga makolo ndi ena makamaka tikakhala pabwino. Galu sauwa fupa lili m’kamwa. -Anthu ena akakhala pabwino amaiwala za umphawi wawo ndipo sasamala za anzawo. Galu ukam’ponyera mafupa, sachoka pakhomo. -Munthu ukakhala woolowa manja kapena wamsangala, anthu satha phazi pakhomo pako. Galu umamudzuma asananye. -Munthu akayamba kuchimwa kapenanso zinthu zikama- lakwika, timafunika kumuthandiziratu zinthu zisanafike poipa. Galu wa mfumu ndi mfumu ya Agalu. -Amene ali m’maudindo ena monga nduna, amaimira mtsogo- leri wamkulu, choncho ngakhale atakhala kuti samatsuka m’kamwa, timafunikabe kumawalemekeza. Galu wadyera (wolusa) anapita ndi goli lake. -Tisamachite chinthu ndi mtima wongofuna kusangalatsa ena 59