Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 57

Miyambi ya Patsokwe Fisi akatola fupa sadyera pomwepo. -Sibwino kumangouza aliyense za mwayi umene tapeza monga udindo chifukwa angayambe kuona kuti ndife onyada. Fisi akazingwa amadya udzu. -Munthu ayenera kumakhutira ndi kangachepe kamene wapeza akakhala pamavuto. Fisi amakhalabe fisi, ngakhale atasintha tchire. -Munthu woipa ndi woipa, sangasinthe chifukwa choti wasintha malo. Chimodzimodzinso chinthu choipa, sichingasanduke chabwino ngakhale utachichita pa zolinga zabwino. Fisi atolapo tsoka. -Munthu ukakhala wakhalidwe loipa monga kuba ndiye chinthu n’kusowa pakhomo, anthu amangoti ndiwe, ngakhale palibe umboni wokwanira wachitadi zinthuzo ndiwe. Fisi ayamika ake maluwa. -Munthu amakonda kuyamikira zinthu zake n’kumaona kuti n’zabwino kuposa zonse. Fisi ndi Mbuzi sizigonera limodzi. -Mawuwa amanena za zinthu zomwe ndi zosayenera kukhalira limodzi kapena kugwirizana. Mwachitsanzo, anthu odana, say- enera kumakhalira limodzi chifukwa mapeto ake akhoza ku- phana. Fisi saopa mdima. -Munthu amene amakonda zoipa saopa anthu kapena zinthu zo- opsa ndi zonyansa. Amayendanso ndi anzake omwe ndi oipa. Fodya amakoma ngokoketsana. -Mawuwa amatanthauza kuti moyo wa munthu umakoma ndi kugawana zinthu monga nzeru, zakudya, zovala ndi zina. 56