Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 56

Miyambi ya Patsokwe Fisi adakana nsatsi. -Si zonse zimene anthu amanenera munthu zimakhala zoona. Ngakhale munthu atakhala wamakhalidwe oipa, pamafunika umboni weniweni tisanamunene kuti wachita cholakwa. Fisi adalira msampha utaning’a. -Nthawi zina timataya mtima kapena kugwa mphwayi mavuto athu atatsala pang’ono kutha. Tiyenera kupirira mpaka pamapeto. Fisi akafuna kuluma sasiya mkute. -Ndi bwino kumangochitiratu chinthu m’malo mosiya zina kuti udzachitabe. Fisi akagwa m’mbuna sayankhula kanthu. -Munthu akapalamula mlandu amafunika kungovomereza ndi kupepesa m’malo momakula mtima. Mawuwa anganenedwenso ngati munthu akusowa choyankhula akagwidwa ndi mlandu. Fisi akagwa m’mbuna, mawa adzalandira nkhwangwa. -Munthu akachita choipa, zivute zitani amakumana ndi mavuto a zimene wachitazo. Choncho ndi bwino kungovomereza ndi kupepesa m’malo momakula mtima. Mawuwa anganenedwenso ngati munthu akusowa choyankhula akagwidwa ndi mlandu. Fisi akagwira sataya. -Munthu suyenera kutaya chinthu chimene umachidalira ko- manso chimakuthandiza monga ntchito, chipembedzo ndi zina. Fisi akakhuta salilira pomwepo. -Pamene munthu wapeza mwayi wina, usamawanyang’wire amene akupatsa mwayiwo monga makolo, aphunzitsi ndi aku- luakulu a pantchito, chifukwa angakulande zomwe wapezacho. 55