Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 55

Miyambi ya Patsokwe Dzungu m’gonera kumodzi. -Mawuwa amanena za anthu omwe amangochita zawo. Safuna kumva za ena kapena kugwirizana ndi anzawo. Dzuwa likawomba, wotheratu. -Mwayi ukapezeka, kapenanso ukakhala ndi nthawi, mpofunika kuchitiratu zowe ukufuna kuchita, chifukwa mwina tsiku lotsa- tira kudzakhala mitambo. Dzuwa likung’amba mtengo. -Mawuwa amanenedwa zinazake zikachitika poyera anthu akuona. Dzuwa likuwomba mtengo. -Mawuwa amanenedwa zinazake zikachitika poyera anthu akuona. Dzuwa limanyenga, mdima umasaka. -Pamene walakwira makolo masana, umatha kuthawa. Koma kukada umapitanso kwa makolo ako n’kukalangidwa. Cholakwa sichithawika, nthawi imafika ndipo munthu ama- landira chilango cha zimene wachita. Dzuwa salozerana, aliyense amaliona yekha. -Pali zinthu zina zomwe sitimafunika kuchita kufotokozera anzathu. 54