Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 54

Miyambi ya Patsokwe ndalama. Amakonda kugwiritsidwa ntchito ndi amwenye omwe amapanga bizinezi. Dziko silimaipa, amaipa ndi anthu. -Tisamaganize kuti tikachoka pamudzi wina n’kupita kwina chifukwa cha kukangana ndiye kuti kukangana kwatha ayi, chifukwa amene amayambitsa kukangana si malo, koma anthu. Dzimvere mtolo. -Mawuwa amanenedwa pouza munthu kuti wamva zimene zanenedwa, kwatsala n’kuti azigwiritse ntchito. Dzina silifa. -Ana akabadwa amatsala ndi dzina la munthu amene ana- wabereka. Dzinena kuti mafano, udzafa maono adakayera. -Mwambiwu umatanthauza kuti kunyoza malangizo a aku- luakulu kapenanso zikhulupiriro zamtundu wako kungakubweretsere tsoka. Mpofunika kumanyadzira chikhalid- we chathu komanso kumamvera malangizo. Dzino siliononga nyumba ya msonkhano, koma lirime. -Chimene chimachititsa kuti anthu asiye kugwirizana kawiri- kawiri silikhala dzino, koma pakamwa. Dzira siliola tsiku limodzi. -Khalidwe la munthu siliyamaipa tsiku limodzi. Ngati munthu walakwa ndiye kuti anayamba kale kuchita zinthu zoipa, kungoti sankagwidwa. Dzungu limakula kunsonga. -Nthawi zina munthu wobadwa pambuyo ndi amene amakhala wamphamvu, wokula bwino ndiponso wanzeru kuposa wo- yamba kubadwa. 53