Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 52

Miyambi ya Patsokwe Dombolo n’kuwombolana, nthengu anaombola namfuko. -Kuti anzako akuthandize pamafunika kuti nawenso uziwathan- diza, osamangoyembekezera kuti anthu akuthandize. Dombolo n’kuwombolana. -Mnzako akukuchitira zabwino nawenso ndi bwino kumuchitira zabwino. Zimakhala bwino kumathandizana. Dothi sinkadakudya, ndakudyera ku uchi. -Nthawi zina umathandiza munthu osati chifukwa choti umamukonda, koma chifukwa choti umakondana ndi mnzake. Dulani kachere pumbwa anyale. -Anthu ena amanyada mwinanso kuzunza anzawo chifukwa cha udindo, ndalama kapenanso makolo awo. Zinthu zotere zikatha, kuzunza ndi kunyada kumathera pomwepo. Dyera linapititsa Ntchentche kumanda. -Kuchita zinthu mwadyera pa chilichonse, ngakhale chabwino, kumatsekereza zabwino, monga kukwezedwa pantchito. Dyeratu, chakudza sichinena. -Munthu ngati uli ndi chuma uyenera kusangalala nacho chifu- kwa zamawa sizidziwika. Dzandioneni n’kukhala ndi zako. -Osamadzitamira katundu wa eni ake koma wako. Dzanja limodzi silikumba mankhwala. -Kuthandizana n’kofunika popeza pawekha sungachite zinthu zambiri. Dzedzeredzedzere (dzandidzandi) salingana n’kugweratu. -Kulephera sikutanthauza kuti sungakwanitse kuchita chinthu. Kuti munthu achite bwino amafunika kukumana kaye ndi mavuto. 51