Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 51

Miyambi ya Patsokwe Dala la mwana wankhuku lolira make ali pomwepo. -Anthu ena amangodandaulabe ngakhale kuti ali nawo anthu owathandiza. Aliponso ena amene amavutika koma njira yothet- sera mavuto awo akuidziwa. Dala lidagoneka munda. -Kulekerera kumawonongetsa zinthu. Ulesi si wabwino mpang’ono pomwe. Dama n’kumeta, mphini ndi chironda. -Pofuna kuwonjezera kukongola kwa chibadwa, nthawi zina ti- madziwononga potsata njira zosayenera. Dengu lidawombola mbiya. -Ndi bwino kumathandizana. Aliyense ndi wofunika pantchito yake. Dengu silidya. -Nsengwa, dengu kapena bwato zimangosunga zinthu zimene mwaikamo, sizimachepa kapena kuwonjezereka. Tizikhutira ndi zimene tili nazo pamoyo wathu. Dikira madzi apite, kenako uziti ndadala. -Munthu ukakhala pabwino usamati ndadala, chifukwa ukhoza kukumana ndi mavuto nthawi iliyonse. Dingudingu amanena za mnzake, zake wapsindira. -Pali anthu ena omwe amakonda kunena zoipa za anzawo n’kusiya zawo. Munthu aliyense amayenera kumayamba waona kaye zimene amachita asanayambe kunena za anzake. Diso la Nkhwazi. -Maso a Nkhwazi ndi akuthwa kwambiri omaona chinthu chili patali. Mawuwa amanena za munthu amene amaona patali. Diso likatuluka, ndi maliro. -Maso a munthu akatuluka, ndiye kuti munthu wamalizika. 50