Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 50

Miyambi ya Patsokwe Chulukechuluke ngwa njuchi, umaloza yomwe yakuluma. -Pokamba nkhani pafunika kunena zenizeni m’malo momango- zungulirazungulira. Mwambiwu umanenedwanso pakakhala anthu ambiri amene akuganiziridwa kuti alakwa, koma pamapeto pake amapezeka m’modzi. Ungatanthauzenso kuti chimene chakudolola n’chimene umachitchula Ungatanthauzen- so kuti chinthu chimene chimakuchititsa chidwi ndi chimene ukuchidziwa bwino. Ngakhale patakhala zinthu zochuluka, umanena za chimene chakuchititsa chidwi. Chulutsa masamba, ungagwire nsete. -Mwambiwu umanenedwa pouza munthu kuti achulutse zonena kuti asagwidwe. Chuma chili m’nthaka. -Ukalimbikira kulima, udzapeza zofuna zako. Chuma chimuka pa chuma chinzake. -Anthu amene ali ndi chuma ndi amene amapeza chuma china. Chuma chothamangira chimapatsa matsoka. -Kususukira kulemera kungatipalasire moto. Chuma ndi mchira wa khoswe, suchedwa kupululuka. -Chuma sichichedwa kutha ngati mmene umachitira mchira wa khoswe. Ukaugwira, umangopululuka. Ngati sukuchisamalira bwino, chimatha chonse phu! Ukakhala pabwino usamanyoze anzako chifukwa ndi amene angadzakuthandize ukadzavutika. 49