Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 49

Miyambi ya Patsokwe wamunthu chifukwa nthawi zina pathawapo umakumana ndi vuto lina lalikulu. Chozingwa sichilira nkhata. -Tikakhala pamavuto pafunika kuyamba kudzithandiza tokha osamangoyembekezera kuthandizidwa ndi ena. Tikadzithandiza tokha enanso adzatha kutithandiza. Chule anadabwa m’madzi muli mwake. -Pali zinthu zina zomwe zimachita kuonekeratu kuti sizimakha- la choncho. Chule anadabwa madzi atafika m’khosi. -Mawuwa amanenedwa munthu akamadabwa ndi zinthu zom- we zimayenera kuchitika pamoyo wathu. Chule wodzikuza adaphulika. -Sibwino kumadzikuza chifukwa umatha kudzichititsa manyazi pagulu. Chulu sichiyendera chiswe, chiswe chimayendera chulu. -Chithu ukachifuna umafunika uchite chinthucho. Chulukechuluke n’ngwa njuchi, umanena za iyo yakuluma. -Pokamba nkhani pafunika kunena zenizeni m’malo momango- zungulirazungulira. Mwambiwu umanenedwanso pakakhala anthu ambiri amene akuganiziridwa kuti alakwa, koma pamapeto pake amapezeka m’modzi. Ungatanthauzenso kuti chinthu chimene chimakuchititsa chidwi ndi chimene uku- chidziwa bwino. Ngakhale patakhala zinthu zochuluka, umanena za chimene chakuchititsa chidwi. Chulukechuluke ngwa chambo, doko n’la ntchira (kambuzi). -Ngakhale ogwira ntchito akhale ambiri, komabe, eni ntchito kapenanso amene akugwira molimbika amadziwika. 48