Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 48

Miyambi ya Patsokwe Chonona chifumira ku dzira. -Maonekedwe ndi makhalidwe a munthu amakhala ochokera kwa makolo ake. Choopera patali, nyani anadzipha yekha. -Si bwino kumangoopera chinthu patali. Chosadziwa anausa mvula m’dziwe. -Nthawi zina tikhoza kumaganiza kuti tikuthawa mavuto n’kud- zilowetsa m’mavuto aakulu mmalo mongopirira n’kuyesa kuthetsa vutolo. Mwachitsanzo, munthu amene wadzimangirira amati akuthawa mavuto. Chosadziwa ndi nkhondo, adausa nkhondo padziwe. -Nthawi zina tikhoza kumaganiza kuti tikuthawa mavuto n’kud- zilowetsa m’mavuto aakulu mmalo mongopirira n’kuyesa kuthetsa vutolo. Mwachitsanzo, munthu amene wadzimangirira amati akuthawa mavuto. Chosamva adachiphikira m’masamba. -Anthu amene samvera malangizo amakumana ndi zokhoma kapena kufa kumene. Wina akakulangiza pamafunika kumvera. Chosatha n’chiyani? -Chilichonse chimatha pakapita nthawi. Chotola salanda. -Kutola kanthu si kuba, koma ukatenga pakhomo pa munthu osapempha. Chozemba chinakumana ndi chokwawa. -N’kovuta kuthawa mavuto kapena milandu chifukwa nthawi zina pothawapo umakumana ndi vuto lina lalikulu. Nthawi zina munthu amazemba, koma tsiku lina amadzagwidwa. Chozemba chinalinda kwawukwawu. -N’kovuta kuthawa mavuto kapena milandu pamoyo 47