Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 47

Miyambi ya Patsokwe Chizolowezi cha namkholowa chidazulitsa mbatata yapansi. -Zinthu zina zimaululika chifukwa cha zinanso zimene zachi- tika. Makhalidwe oipa monga chiwerewere ndi kuba amayamba pang’onopang’ono. Pamafunika kudziletsa kuti usachite zinthu zomwe mapeto ake akhoza kukhala kuchimwa kwakukulu. Chizolowezi chidadya mzuzya. -Zotsatira za zizolowezi zoipa ndi mavuto monga matenda, milandu komanso imfa. Chizolowezi chinalowetsa nsabwe kumutu. -Ukamacheza ndi anthu ochita zoipa nawenso umayamba ku- chita zoipa. Choipa chitani mbiri siigonera. -Mbiri imamveka msanga. Ngakhale utayesetsa kuimphimba an- thu amamva. Koma sipapita nthawi amayamba kuiwala. Choipa chitsata mwini. -Palibe munthu amene angachite choipa n’kuthawa, tsiku lina ndithu amadzakumana ndi zotsatira za zoipa zimene anachi- tazo. Choipa ndi mnyanga ya njovu. -Munthu ukhoza kumachita zoipa n’kumaganiza kuti sichidzau- luluka. Koma monga mnyanga ya njovu sitheka kuibisa, choipacho tsiku lina chimadzaululika ndipo munthu umadzalangidwa. Choka m’mbuyo Khwangwala atole mphutsi. -Umafunika kupereka mpata kwa anzako kuti akhale omasuka pang’ono. Osamatsekereza mwayi wa ena. Cholira Njovu chidalira minyanga. -Aliyense ali ndi ufulu wogwira ntchito imene akufuna popanda kukakamizidwa. 46