Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 46

Miyambi ya Patsokwe kuwathandiza zili m’nkhonde. Mwachitsanzo, kumavutika ndi njala dimba ali nalo. Chitsiru chinaomba ng’oma, ochenjera navina. -Nthawi zina anthu ooneka ngati opusa ndi ofooka amatha ku- chita zodabwitsa motero kuti anthu odziyesa ochenjera n’kuten- gerapo phunziro. Chitsiru chinaona nkhondo. -Si bwino kunyoza munthu chifukwa santha kuchita zinthu zina. Nayenso akhoza kukhala ndi mbali ina yomwe amachita bwino. Chitsiru nachonso chili ndi amake. -Ana kapena ziweto zimadziwa makolo komanso mbuye wawo. Munthu sulephera kuzindikira chinthu chako. Chitsulo chimanola chitsulo chinzake. -Anthu ochita zofanana amathandizana. Kuti munthu akhale ndi luso amayenera kumatengera anzake. Chitukuko ndi kupirira. -Kuti atsikana kapena azimayi atchene, kaya ndi m’mutu, ama- funika kupirira ululu. Mwachitsanzo, ena amapsa ndi livuloni koma samasiya. Chiwindi cha Nkhandwe chalaka mwini msampha. -Chomwe chakanika munthu wakale kapena wanzeru, mwana sangachithe. Chiyipira achaje, amake amati mwana. -Ngakhale anthu ena atamanyoza munthu chifukwa cha maon- ekedwe kapena khalidwe lake, makolo ake ndi abale ake ama- mukonda, sangamutaye kapena kumunyoza. Chizolowezi cha namkholowa chidaululitsa mbatata. -Si bwino kuchita khalidwe loipa chifukwa likhoza kukubwer- etsera mavuto. 45