Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 44

Miyambi ya Patsokwe Chisoni chinapha Nkhwali. -Nthawi zina chisoni chikhoza kukubweretsera mavuto. Nkhani yake imati, kalekalelo Njoka inkafuna kuwoloka mtsinje wina. Ndiye popeza palibe chimene ikanachita kuti iwoloke yokha, inapempha Nkhwali kuti aithandize. Nkhwaliyo inamva chisoni zedi ndi mmene Njokayo inkaonekera ndipo inavomera kuti ichitadi zimene Njokayo inkafuna. Inauza Njokayo kuti, “Zizengereze m’khosi mwangamu!” Kenako inanyamuka n’kuuluka. Itafika kutsidya, Nkhwaliyo inauza Njokayo kuti, “Bwanawe, tafikatu. Tsopano ukhoza kutsika kuti uzipita.” Koma Njokayo inakana kwamtuwagalu kuti sichoka. Pamapeto pake, chisoni chinachitsa kuti Nkhwali ione tsoka la nkhuku. Chisoni chinapha nsemamitondo. -Munthu amene umamuthandiza poganizira kuti akusowa thandizo ndi amene amadzakuukira, mwinanso ngakhale kuku- pha kumene. Chisoni n’kumatenda, kumaliro kumakhala nkhani. -Pamene munthu akudwala anthu amakhala ndi chisoni, koma akamwalira, chisoni chonse chimatha popeza amadziwa kuti palibenso chimene angachite. Mwina ena amayamba kukamba mbiri ya womwalirayo, zabwino kapena zoipa. Chiswe chikaboola chikwa, chayambira patali. -Munthu ukakhala ndi cholinga n’kuchita khama, umapeza zimene ukufuna. Ungatanthauzenso kuti vuto likamaonekera ndiye kuti layambira patali. Chiswe chimalowa m’mphasa yongoimika. -Munthu waulesi amakumana ndi zovuta zambiri. Chiswe chimodzi sichiumba chulu. -Ngati titamathandizana tikhoza kugwira bwino ntchito zathu mpaka kumapeto. 43