Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 40
Miyambi ya Patsokwe
chifukwa tikamatero tikhoza kuiwala zinthu zofunika.
Chimanga cha palikodza amakolola ndi Sakhwi.
-Ndi bwino kumadziwa zinthu zomwe sungakwanitse. Pali zin-
thu zina zomwe ngati utazikakamira kwambiri zikhoza
kungokubweretsera mavuto ngati chimanga chomwe chili pali-
kodza, lomwe ndi tchire loyabwa kwambiri. Ndi bwino kusiyira
Asakhwi zinthu zimenezo.
Chimanga chimalola opanda mano.
-Nthawi zina munthu umapeza chinthu choti ulibe nacho ntchi-
to pamene munthu wina akuchifunitsitsa.
Chimasomaso chinakwatitsa mkazi wosam’funa.
-Mnyamata wosakhala ndi mkazi m’modzi koma kumangoti apa
wagwira apa wagwira, mapeto ake amadzakwatira mkazi wosa-
khala wakumtima kwake, mwinanso kupeza mavuto.
Chimene chakupundula chitsate, chikupatsa khongozo.
-Munthu uyenera kudyerera chomwe wavutikira.
Chimene ukufuna kuti ena akuchitire, iwenso uziwachitira
chomwecho.
-Kuti tizichitira ena zabwino, ndi bwino kumayamba taganiza
kaye kuti, “Kodi wina atandichitira zimenezi ndingasangalale?”
Ngati tikuona kuti sitingasangalale, tingachite bwino osazichita.
Chimkonda cha nsikidzi chidanka ndi maliro kumanda.
-Osamakonda zinthu zoipa monga chiwerewere, mowa kapena
chamba chifukwa mapeto ake ndi imfa.
Chimkwangukwangu chisititsa makadabo.
-Kulimbirana zinthu kukhoza kuyambitsa ndewu kapenanso
mkangano n’kuwonongetsa zinthu zambiri.
Chimuyesoyeso cha Khwangwala chinathetsa ana.
-Si bwino kuyesa kuchita zinthu zoipa monga kusuta chamba
39