Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 39

Miyambi ya Patsokwe lakelo n’kuliika munkhali n’kutenga madzi obwadamuka n’ku- wakhuthulira momwe munali bulangetelo kuti nsikidzizo zikhaule. Ndiye zimenezi zitangochitika, Nsikidzi yomwe inali m’bulangetemo inauza ana ake kuti, “Ana anga, muyenera ku- khala opirira, chifukwa chilichonse chotentha, pamapeto pake chimazizira. Vuto lingatenthe bwanji, limakhala ndi mapeto ake.” Mavuto angakule bwanji, amakhala ndi polekezera. Chilimwe chinaphetsa munda. -Munthu wofuna zabwino asamathawe zopinga monga kuuma komanso kulimba kwa dothi, amafunika kupirira. Chilimwe, ndipatse munda. -Munthu akafuna kuti adzapeze zabwino m’tsogolo amafunika kukonzekera. Chiloli chinapha ngondo. -Ukakhala munthu wachidwi ndi wofuna kudziwa chilichonse, tsiku lina umadzakhala mboni pa mlandu woopsa, mwina n’kupeza mavuto. Chilosi chidabwerera lunguzi. -Mukanyoza munthu osam’patsa moni chifukwa choti ndi mlen- do, tsiku lina mumadzakam’peza kwawo n’kuchita manyazi. Chilungamo chiziyenda ngati madzi. -Chilungamo chimafunika chioneke. Tikamachita zinthu zonse, tiyenera kumaonetsetsa kuti tikuchita zinthu mwachilungamo kwa aliyense mosatengera maonekedwe. Chilungamo n’chipongwe. -Nthawi zina anthu amadana ndi kumva chilungamo chifukwa chimamveka ngati chipongwe. Chim’mawa chidalambalalitsa fulu bowa. -Tizichita zinthu mofatsira ndi mwaluso osati mongofulumira, 38