Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 38

Miyambi ya Patsokwe mavuto a mnzako. Chili kwa mnzako ndiye “psinyitsa,” chili kwa iwe ndiye, “psinya bwino.” -Mnzathu akalakwa ndiye timafuna kuti alandire chilango chowawa, koma zikakhala kwa ife, timafuna kuti atimvere chi- soni potipatsa chilango chofewa. Chili kwa mnzako umati “chigwire nyanga!” -Munthu amaona vuto la mnzake ngati si vuto ayi, koma vuto ngati lomwelo likamuonekera m’pamene amaliwona kuti ndi phiri. Chili kwa mnzako, utenga madzi numwera. -Mavuto akakhala kwa ena kumakhala kosavuta kuwalangiza zomwe anachita kuti apeze mavutowo, koma zikatigwera sititha kumvetsa chomwe chachititsa mavutowo. Chili kwa nyani, pusi sachitengera malonda. -Nthawi zambiri pakati pa abale sipakhala kugulitsana zinthu koma kungopatsana basi. Chili n’kudza chisonkha moto paphale, chipala (phulusa) chi- taya kuthengo. -Mawuwa amanenedwa munthu akamanena kuti alipo wina womuposa amene akubwera. Chilichonse chili ndi nthawi yake. -Ndi bwino kumachita zinthu pa nthawi yake. Kumadziwa nthawi yabwino yochita chilichonse monga kuyankhula kapena kukhala chete. Chilichonse chotentha, pamapeto pake chimazizira. -Munthu wina atatopa kulumidwa ndi Nsikidzi, anaganiza zotereka madzi kuti azikhaulitse. Kenako anatenga bulangete 37