Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 37

Miyambi ya Patsokwe kugwira ntchito inayake, tsiku lina pamadzakhala china chotik- umbutsa chomwe tinaiwala. Nthawi zina mavuto amatichititsa kugwira ntchito molimbika komanso kugwira ntchito zomwe tinkaziona ngati zopanda pake. Chikuni cha m’bwalo chikoma n’kugwirizana. -Kuthandizana n’kofunika kwambiri m’malo momadzipatula. Chikuni cha utsi timafumula. -Pakakhala munthu wosokoneza pamudzi kapena pantchito pa- mafunika kumulangiratu kuopa kuti angasocheretse ena. Chikuni chimodzi sichipsetsa mphika. -Kuti ntchito iyende pamafunika kuthandizana. Chikuni pakutha, chimataya therere. -Nthawi zambiri ntchito imaonongeka kumapeto. Ndi bwino kumasamala pogwira ntchito mpaka kumapeto. Chilekwa (wamasiye) n’chosakhala kupatira chabwino. -Nthawi zina mwana wamasiye amatha kupeza msanga chithandizo. Zinthu zonyozeka zingathe kutipatsa zabwino. Chilendo ndi kulumpha chiunda. -Munthu ukangotuluka m’nyumba mwako kwina konse uma- khala mlendo. Chili kumunda n’chambewu, chakumudzi n’chakudya. -Tizisunga zina kuti tidzagwiritse ntchito m’tsogolo. Chili kumwamba ndi chamwini. -Si bwino kukhumbira zinthu za eni kapena zinthu zomwe tikudziwa kuti sitingathe kuzipeza. Chili kwa mnzako n’kumati, “chigwire nyanga.” -Sizivuta kupeza zolakwa za mnzako n’kusiya zako kapena kuu- za ena zoti achite koma zoti iweyo sungakwanitse. Osamaderera 36