Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 36

Miyambi ya Patsokwe Chikondi chili m’manja. -Mawuwa amanenedwa pofuna kuonetsa kuti umafunitsitsa utakumana ndi mnzako n’kumupatsa moni. Chikondi ndi kutherana zakukhosi. -Chizindikiro cha chikondi chenicheni ndi kuululirana zaku- khosi, osati kusungirana chakukhosi. Chikumbumtima chinapha njovu. -Tikachita choipa chikumbumtima, chomwe ndi munthu wam’kati, chimatiimba mlandu ndipo timasowa mtendere. Chikumbumtima chikhoza kumakupwetekabe ngakhale utafun- da mabulangete ambirimbiri. Ndi bwino kumavomereza tikala- kwitsa ndi kupempha kuti atikhululukire. Nkhani yake imati, tsiku lina njovu inatenga katundu wa mwini wake. Ndiye kalulu ataifunsa inakana kuti sinatenge. Kenako kalulu anauza njovuyo kuti, “Ngati mwatengadi ndi inuyo n’kumakana, chikumbumti- ma chikuphani.” Njovu inayamba kuchita mantha kwambiri chifukwa inkaganiza kuti chikumbumtima ndi nyama ina yai- kulu kwambiri kuposa iyoyo. Njovuyo inasiya kutuluka panja kuti ikasake zakudya mpaka inaonda kwambiri. Inkaopa kuti ikumana ndi chikumbumtima. Kenako njovuyo inafa ndi njala. Phunziro lake ndi lakuti ndi bwino kumavomera ukalakwitsa, chifukwa ukapanda kutero umavutika ndi chikumbumtima. Chikumbutsa nkhwangwa n’chikuni. -Ngakhale tiiwale kanthu kena kapena kuchita mphwayi kugwira ntchito inayake, tsiku lina pamadzakhala china chotik- umbutsa chomwe tinaiwala. Nthawi zina mavuto amatichititsa kugwira ntchito molimbika komanso kugwira ntchito zomwe tinkaziona ngati zopanda pake. Chikumbutsa nkhwangwa n’chisanu. -Ngakhale tiiwale kanthu kena kapena kuchita mphwayi 35