Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 35

Miyambi ya Patsokwe Chikakuluma chakuda umaopa ndi khala lomwe. -Munthu wina akakupusitsa, sukhulupirira aliyense. Chikaona mnzako osamaseka. -Mnzako akaona tsoka usamamuseke chifukwa mwina mawa udzaonanso zomwezo. Chikaonda chimakoma ndi mchere. -Chinthu chingakhale choipa maka, koma powonjezera tina n’ti- na tokometsera, chinthucho chimakhalanso chokongola. Chimodzimodzi mkazi amaoneka bwino ndi kuvala. Chikaonekera ng’amba, mawa chituluka. -Mbewu ikamamera imayamba yatukula dothi kenako n’kuon- ekera. Zinthu zina zikamaoneka pamakhala pataoneka kale zizindikiro zake. Chikomekome cha mkuyu, m’kati muli nyerere. -Osamatengeka ndi maonekedwe a munthu chifukwa nthawi zi- na mumtima mumakhala moipa. Nthawi zambiri anthu okongo- la ndi amene amakhala a makhalidwe oipa. Chikondi cha “chotsa phazi mpondepo.” -Chimenechi ndi chikondi chenicheni chochitira zinthu limodzi. Chikondi cha bulangete chopitira limodzi kumanda. -Chikondi chopanda chinyengo komanso dyera, chokhalira limodzi pamavuto ndi pamtendere pomwe. Chikondi cha chotsa phazi m’pondepo. -Chikondi chodalirika kapena chokondana kuchokera pansi pa mtima. Chikondi cha mphaka, chobisa zala m’thumba. -Chikondi chobisilana cholinga chako chenicheni. Chikondi chachinyengo. 34