Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 33

Miyambi ya Patsokwe akhoza kuoneka ngati sakuganiza chilichonse koma akuganiza zambiri. Munthu aliyense amadziwa yekha zinthu zimene an- gakhutire nazo. Chidziwe n’chipande powomola. -Aliyense amakolola malinga ndi khama lake. Munthu akady- eratu kapena akamachita ulesi, amalandira zochepa. Chifuko sakumbira. -Chibale chenicheni sichisowa. Chifulumizo chokoma ukalasa. -Tiziganiza mofatsa tisanayankhe chifukwa tikhoza kuyankhula zopanda pake. Komanso munthu umakamba mosangalala ukamachita zinthu zabwino. Chifundo chidaphetsa msemamitondo. -Chifundo nthawi zina chimapweteketsa. Nkhani yake imati, nthawi ina alenje anavumbulutsa gondwa ndipo anayamba ku- muthamangitsa. Alenjewo anamupezeketsa gondwayo moti anangotsala pang’ono kumugwira. Gondwayo anayesetsa kuko- ka phazi koma sizinam’thandize moti anaganiza zopempha thandizo kwa munthu wina yemwe ankasema mitondo m’nk- halangomo. Atatoperatu, gondwayo anapempha wosema mi- tondoyo kuti, “Ndithandizeni chonde ndagwira mwendo wanu. Alenjewa akufuna moyo wanga, chonde ndipulumutseni!” Wosema mitondoyo anamva chisoni kwambiri ndipo anauza Gondwayo kuti amubisa. Koma popeza panalibe malo pafupi pomwe akanamubisapo, wosema mitondoyo anangoganiza zomubisa m’kamwa. Alenjewo atafika anafunsa wosema mi- tondoyo kuti, “Mwaona Gondwa atadutsa apa?” Koma wosema 32