Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 32

Miyambi ya Patsokwe wapulumuka pa vuto mwamwayi, si bwino kubwereza ku- chitanso zomwezo. Chidakwa chinakana kulipira ngongole ya thobwa. -Si bwino kumangonamizira anthu amene tikuwaona kuti ndi zitsiru kapena opepera. Chidamlendo mbombo. -Munthu woti akakhala ndi chakudya sakonda kugawira anthu ena. Chidebe chopanda kanthu n’chimene chimasokosa kwambiri. -Anthu opanda nzeru ndi amene amakhala olongolola kwambi- ri. Chidede kukanika chitayang’anana. -Ndi bwino kumayesetsa kuchita khama pochita zinthu. Zichite kukanika zokha. Chidule chimapondetsa matope. -Zinthu zochitika mofulumira kapena mwachidule sizichitika bwino. Chidule chinagwetsa njati m’mbuna. -Si bwino kuthamangira kapena kuchita zinthu usakudziwa ndondomeko kapena dongosolo lake chifukwa zimenezo zikho- za kukubweretsera mavuto. Chibwana cha nyani chokhalira msampha mtengo nawuona. -Chibwana chachikulu chomwe chikoza kukutsayitsa zambiri. Chidwi chinapha mkonzi. -Ukakhala munthu wachidwi ndi wofuna kudziwa chilichonse, tsiku lina umadzakhala mboni pa mlandu woopsa, mwina ukhozanso kupeza nazo mavuto. Chidziwa mwini m’khuto wa fulu. -N’kovuta kudziwa zomwe munthu akuganiza mumtima. Ena 31