Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 31

Miyambi ya Patsokwe zimawalowetsa m’mavuto. Chibwana ndi chironda. -Mwana sachedwa kuvulala chifukwa alibe mantha. Ndiye mun- thu wachibwana, kapena wosalemekeza akuluakulu amapeza mavuto. Chibwenzi cha bulangete chopitira limodzi kumanda. -Umenewu ndi ubwenzi weniweni, wopanda chinyengo. Chibwenzi cha mphaka chobisa zala m’thumba. -Pali anthu ena omwe amaoneka ngati abwenzi pamaso koma kumbali amakuganizira zoipa. Chibwenzi cha nkhwangwa chikoma pokwera. -Pali anthu ena omwe amakonda anzawo akaona kuti akhoza kuwathandiza, akangopeza zimene amafuna ubwenzi umathera pomwepo. Chibwenzi cha nkhwangwa chokoma pokwera, potsika achita kuponya. -Munthu akamakwera mumtengo amanyamula bwinobwino nkhwangwa koma akamatsika amangoiponya. Mawuwa amanenedwa munthu akamanyoza anzake chifukwa choti zimene umafuna zatheka. Munthu ameneyo amamuti wachita, “chibwenzi cha nkhwangwa chokoma pokwera.” Chibwenzi n’kuwonjezera. -Kupatsana mphatso n’kumene kumalimbitsa ubwenzi. Chibwenzi sichipherana makoswe. -Ubwenzi weniweni ulibe chinyengo. Chomwe wamuuza kapena wam’lonjeza mnzako chimakhala chomwecho. Chibwereza chidaphetsa kunda. -Munthu ukamachita chinthu choipa n’kupulumuka, tsiku lina ukamadzati uchitenso anthu amadzakugwira. Ngati munthu 30