Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 283

Miyambi ya Patsokwe “Zikubwerera” anafa ndi linthumbu. -Ukamachitira anzako zoipa, zomwezo zimadzakuchitikira iweyo. “Zili konku,” kudya kwa Awiza. -Mawuwa amanena kuti tizidya mofanana ngakhale ndisa- chitepo kanthu. “Zili kwa amchira,” gondwa ali m’mphako. -Mawuwa amanenedwa pokhana kukhudzidwa ndi zinthu kapena nkhani za ena. “Zili uko” adabwera chaje osatenga nsomba. -Tisamatengeke ndi zinthu zongomva koma tizifunsa kuti tidzi- we chochita. Ngati munthu wina anaona nsomba osafunsa n’kupezeka wabwera chimanjamanja. “Zili uku” anathyoletsa mwendo. -Munthu wina anathyoka mwendo pothamangira zongomva chabe. Tidziyamba tafunsa kuti tidziwe mmene zilili osaman- gomvera zilizonse zomwe ena akunena. “Ziliko” n’kulinga utatosako. -Ndi bwino kukhala ndi umboni weniweni pa zimene tamva ti- sanayambe kuchita zinthu. “Ziri bwino momwemu,” anakhalitsa tsindwi pakhudu. -Pakhudu ndi pambali. Munthu wina anzake ankamuthandiza kuika denga pankhokwe yake. Ndiye anangoyankha mopupu- luma kuti ziri bwino momwemu ndipo denga lidakhala pamba- li. Anthu ena samaika mtima wawo pantchito, choncho amachita zosalongosoka ntchitoyo n’kuwonongeka. Ena akabwera amachita kudzayambiranso poyambirira. 282