Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 282
Miyambi ya Patsokwe
“Timwenji ife,” dzungu n’gonera kumodzi.
-Munthu angayankhule mawu amenewa podandaula kuti alibe
anzake omwe angamamuuze nkhani za pamudzi.
“Tidzaona mawa” anagoneka munda.
-Si bwino kumachita zinthu mozengereza. Ndi bwino kumachita
zinthu pa nthawi yake ngati tikufuna zitiyendere.
“Tiyenitiyeni” sachoka, achoka ndi vundumu.
-Kungonena mawu okha sikupindula koma kuchita.
“Tizimve,” mwana wakwathu ali komweko.
-Ngakhale akufuna kubisa tidzamvabe chifukwa anthu amene
ali kumeneko ndimadziwana nawo.
“Ukaphaneni” suchedwa kulekanitsa mabwenzi.
-Ngati anthu ogwirizana amamvera kwambiri zonena za anthu,
ubwenzi wawo umasokonekera.
“Ukutisokosera” n’kulinga utamva.
-Tisamadalire zonse zomwe anthu akutiuza.
“Usakanene” ndiye adanena.
-Osamakhulupirira anthu chifukwa sasunga chinsinsi. Ukauza
munthu kuti asunge pakamwa mpamene amaulula.
“Vinavina” savinika.
-Si bwino kumakakamiza ena kuchita zimene sakufuna.
“Wandiona bwanji?” palibe mlandu wa maso.
-Chilichonse chinapangidwa kuti chigwire ntchito yake pa
nthawi yakenso.
“Zidzalezidzale” adalinda chiswe.
-Poyembekezera kuti dengu lidzadze, chiswe chinadya dengulo.
Tizichita zinthu mwachangu popewa zinthu zimene zingatileph-
eretse.
281