Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 280

Miyambi ya Patsokwe “Pangapanga” sapangika. -Kungonena kapena kukalipira anthu sikutanthauza kuti ntchito ichitika. Pogwira ntchito pamafunika kukambirana komanso kuthandizana. “Pano mpakwathu” adagona ndi njala. -Osamadalira ena kuti atipatsa zimene tikufuna chifukwa mwina sangatipatse ndiye tingavutike. “Pano mpathu” n’kulinga utakhuta. -Kuti munthu usangalale kapena uzichita zina momasuka uma- funika kudya kaye mokwanira. Koma kuti chakudyacho chipezeke umafunika kugwira ntchito. Munthu amamera mizu pamalo ngati pali chakudya chokwanira. “Pano ndi panga” adakazinga chimera. -Osamadalira ena kuti atipatsa zimene tikufuna chifukwa mwina sangatipatse ndiye tingavutike. “Patse” samatula chiluli, amatula chiluli ndi “taona apa.” -Munthu wopempha amatha kugwiritsa ntchito zimene wap- atsidwa mwanzeru pomwe munthu wakuba amangogwiritsa ntchito zimene wapezazo mosasamala. “Patsepatse” n’kulanda, munthu woolowamanja amadziwa yekha. -Ngati munthu safuna kupereka asanapemphedwe, amaonedwa kuti ndi womana. Ena ukawapempha amangoperekera manyazi. Mwambiwu umatanthauza kuti munthu azipereka mwa kufuna kwake osati kuchita kumukakamiza. “Pepani” sapoletsa chilonda. -Kupepesa ukalakwa kapena ukawononga chinthu chamwini sikukonza zinthu, koma kuchitapo kanthu monga kubweza zimene zawonongekazo. 279