Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 279

Miyambi ya Patsokwe “Ndikupha mawa” sali patali. -Ena akatiuza kuti tidikire, tisamanyinyirike chifukwa nthawi sichedwa kutha. Chachikulu n’kudikira kuti winayo akwaniritse lonjezo lake. “Ndili ndekha ndili ndekha” ndi amene akutha anthu. -Anthu omwe alibe ana ndi amene amachitira ana a ena nkhan- za. Ena omwe alibe katundu amabera anthu ena. “Ndimam’khulupirira” anam’goneka pabwalo. -Pochita zinthu si bwino kumadalira ena kuti adzatithandiza. Munthu wina ankayembekezera kuti mnzake akumudziwa ndipo amupatsa malo ogona. Zitalephereka anagona panja. “Ndimo alili” n’kulinga utamuona. -Kuti udziwe khaliwe la wina umayenera kukhala naye, m’malo mongogamula kuti ndi woipa. “Ndipatendipate” anapata bala. -Ukamapupuluma kuti upeze zinazake umakumana ndi mavuto. “Nyemba zowola udya chaka chino” n’kulinga uli nazo. -Munthu sadandaula akawaputa yekha mavuto. “Nyemereko” adataya nsima kudzenje. -Pali anthu ena omwe amafuna zonse zikhale zawo moti sasan- galala ena akapeza zawo. Munthu womana amatha kuwononga zinthu n’cholinga choti asapatse ena. Mwachitsanzo, pobisa kupezeka kuti zawonongeka. “Pali chikomere” adasiya chikho pabwalo. -Munthu akamaumirira kuchita zoipa amadzasiya chikho pakhonde, amamwalira n’kusiya zomwe ankakondazo. 278