Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 278

Miyambi ya Patsokwe tsiku lina. “Ndidyeretu” adasowa mbewu. -Tisamatsiriziretu katundu kapena mbewu zonse. Tizisunga zina kuti zidzatithandize m’tsogolo. “Ndifa, ndifa” adalaula moyo nthawi yaitali. -Tisamapange malonjezo opanda pake. “Ndikanakhala ine” anathawitsa anyani a mwini wake. -Mawuwa amanena za munthu womva zayekha, wopereka malangizo osathandiza kapena wosowetsa anzake mtendere. “Ndikanakhala ine” sapita kumilandu. -Pali anthu ena omwe amati zinthu zikadutsa amayamba kunena maganizo awo koma pamene zimachitika anangoti du. Kuchita zimenezi sikuthandiza. “Ndikhale nawo” analanda malo. -Alendo ena amakhala ndi cholinga cholanda malo, moti muka- panda kusamala amapezeka kuti ayamba kukulamulirani. Chitsanzo ndi bonongwe. Amayamba ndi m’modzi koma ke- nako amadzadza munda wonse. “Ndikometsendikometse” ndiko kuipitsa. -Osamachita zinthu chifukwa chongofuna kuyamikiridwa, mapeto ake umalakwitsa kapena kuwononga zinthu. “Ndikonzendikonze” adanyula mtembo wa eni. -Si bwino kumachita phuma pa zinthu chifukwa umatha kupal- amula nazo. “Ndikudziwa kale” adamanga nyumba yopanda khomo. -Munthu amene amadziyesa wodziwa zonse amalephera kufun- sa ena, mapeto ake amalakwitsa anthu n’kumuseka. Ndi bwino kumafunsa ena. 277