Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 277

Miyambi ya Patsokwe “Ndakhupuka” adagwetsa nyumba. -Si bwino kumadzitama ndi zimene tili nazo chifukwa sitidziwa za mawa. “Ndakulapa” n’kulinga utayenda naye. -Kuti munthu udziwa khaliwe la mnzako umayenera kukhala naye pafupi osati kungomuona. “Ndakuona” adalasa galu. -Munthu wina ali kosaka nyama anzake anamufunsa ngati waio- na nyama. Iye anangovomera chifukwa ankaona kuti achita manyazi ndipo anagenda n’kupha galu wake yemwe. Ngati sukudziwa zinazake si bwino kungovomerera manyazi. Ndi bwino kupempha ena kuti atithandize. “Ndakwatira” n’kulinga utagonera. -Osamafulumira kunena kuti wapeza banja labwino mpaka patatha nthawi ndithu, chifukwa anthu ena amabisa khalidwe lawo poyamba. “Ndaonera momwemo,” mwambi wa gulugufe. -Tsiku lina gulugufe ankamwa timadzi ta m’maluwa. Ena pomu- funsa anati: “Kodi ukhuta timadzi tomweto?” Gulugufeyo anayankha kuti, “Ndaonera momwemo” kutanthauza kuti nda- vomera zonse zimene mukunenazo. Mawuwa amatanthauza kuti tizikhutitsidwa ndi zimene tili nazo ngakhale ena atama- khamba kuti sangathe kukhala moyo wachoncho. “Ndapakonda” adasiya khonde. -Ukakhala mlendo uyenera kudziwa nthawi yochoka chifukwa ukakhalitsa eni ake amatopa nawe ndipo amasiya kukusamalira ngati mlendo. “Ndichite bwino,” gondwa anafa. -Munthu wochita zinthu modzitama, amadzachita manyazi 276