Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 276

Miyambi ya Patsokwe “N’chomwecho” chidaletsa Nkhandwe kubwera kumudzi. -Nkhandwe imakonda moyo wakutchire. Munthu azichita zin- thu zimene zimamukomera. “N’dzalemera” adamka ndi nguwo ya insa. -Osamazengereza kugwira ntchito chifukwa ukakhala waulesi umangosaukirasaukirabe mpaka kufika povala chikopa cha insa. “N’konzen’konze” adanyula maliro a eni. -Munthu usamajijirike pa zinthu za eni chifukwa ukhoza kupeza mavuto ngati utalakwitsa chinachake. “N’konzen’konze” adasupula mtembo wa eni. -Si bwino kumachita phuma pa zinthu chifukwa umatha kupal- amula nazo. “N’kulen’kule” adagwa padzala. -Kuthamangira kudziwika kumagwetsera munthu m’mavuto. “N’kulendinen’kulendine” adagwa padzala. -Munthu wodzikuza komanso wonyada, anthu ena ama- muchepetsa n’kumuchititsa manyazi. “N’tapen’tape” adataya lipande. -Timafunika kuchita zinthu mwachifatse, osapupuluma chifu- kwa ukapululuma umawononga zinthu ngati munthu amene akufuna kuchotsa lipande (mphale) mumtondo n’kumachita mwachangu kwambiri amataya mphale yambiri. “Ndafulumira” adadya zosapsa. -Tisamachite zinthu mofulumira kwambiri chifukwa pamapeto pake zimakhala zosalongosoka. Tisamafotokoze nkhani yomwe sitinaimvetse bwino, chifukwa tingafotokoze zosapsa. “Ndafulumira” anasiya tonde m’khola. -Changu nthawi zina chimawononga zinthu monga munthu amene sanatsegulire ziweto zake. 275