Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 275

Miyambi ya Patsokwe pomwepo. “Kwazizira” alibe mpani. -Munthu waulesi amakhalanso ndi njala. Tiyenera kugwira ntchito kuti tipeze zimene tikufuna. “Mbewa zidyana,” amatero Aphiri pofunsira Naphiri. -Mawuwa amanenedwa ngati anthu a pachibale akuchita zosay- enera pophwanya chikhalidwe chawo monga pankhani ya kuk- watira. “Mchakwawo” adanka ndi madzi. -Tisamalekerere anthu akuchita zoipa kapenanso akusochera pongoganiza kuti adziwa chochita popeza ndi aakulu msinkhu kapena ophunzira kwambiri. Mpofunika kuwachenjeza ndi ku- wathandiza kuti asagwere m’mavuto. “Momwemo” walinga utamwamo. -Kuti munthu udziwe zinthu, umayenera kuzichita kaye. “Mpokoma pano” ndiye kuti mwagona awiri. -Kuti munthu uyamikire kuti pamudzi kapena pakhomo ndi pabwino, umayenera kucheza ndi ena n’kumva za anthu a pakhomopo. “Mulungu akundiona” anadyedwa ndi ng’ona. -Mulungu amathandiza munthu yemwe amadzithandiza yekha. “Muonere ine” adadyedwa ndi ng’ona. -Si bwino kumadzionetsera kuti timadziwa zinazake, chifukwa tikhoza kupeza mavuto. “Mwana wa a uje wasamba” n’kulinga atakhuta. -Ngati mwana wasamba m’manja atadya ndiye kuti wasangalala ndipo wakhuta. Tizipatsa ana zinthu zokwanira kuti azisangala- la. 274