Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 274

Miyambi ya Patsokwe kumusangalatsa komanso kumulangiza. Pawekha sungachite kalikonse. “Ili kutali mvula,” m’mera uona ng’amba. -Mawuwa amagwiritsidwa ntchito pamlandu ngati mboni yachedwa. Mboniyo ikachedwa, mlandu umayambikabe. Aka- bwera, adzapereka umboniwo panthawi yake. Mwambiwu umalimbikitsa anthu kuti azichita zinthu pa nthawi yake. “Ili kutali mvula,” mpesa umera m’ngamba. -Zinthu zimachitika panthawi yake mosatengera kuti wina kapena chinachake palibe. “Ine panalibe” adang’amba thumba. -Kumvetsera ena akamakufotokozera zimene zinachitika iwe kulibe n’kothandiza kuti usanene kapena kuchita zinthu zomwe sumayenera kuchita. “Izo zokha ndiye ayi,” fisi adakana nsatsi. -Si zonse zimene anthu amanenera munthu zimakhala zoona. Ngakhale munthu atakhala wamakhalidwe oipa, pamafunika umboni weniweni tisanamunene kuti wachita cholakwa. “Kakadachepa,” n’kuona msandulizo. -Tizipempha thandizo kuchoka kwa anzathu zinthu zisanafike poipa. “Kwapita apongozi,” n’kulinga utawaona. -Umayankhula za chinthu chimene wachiona kapena ukuchidzi- wa. “Kwaya kwaya” ndi uchitsiru, wochifuna apempha yekha. -Osamakakamiza munthu kuchita zimene sakufuna. “Kwaya kwaya” wam’kamwa, mtima uli pomwepo. -Mawuwa amanena za munthu amene amalonjeza kukupatsa chinthu asakufuna kukupatsa kapena mtima wakenso uli 273