Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 273

Miyambi ya Patsokwe “Gona n’kuphe” sali patali! -Ena akatiuza kuti tidikire, tisamanyinyirike chifukwa nthawi sichedwa kutha. Chachikulu n’kudikira kuti winayo akwaniritse lonjezo lake. “Gona” ndi mwini nyumba (mudzi). -Ukakhala mlendo sungachite kapena kutenga kalikonse, pokhapokha eni pakhomopo atakuuza. “Gona” ndi mwini wake wa nyumba. -Ulamuliro wa chinthu umayenera kuchoka kwa mwini wake chinthucho. “Ichi chakoma, ichi chakoma,” pusi adagwa chagada. -Osamangotengeka ndi chilichonse koma kumaika mtima pa- chinthu chomwe ukufuna. Ukamati uku wapita, uku wapita, mapeto ake umalephera zonse. “Ichi chakoma,” adagona m’khufi atafika kwawo. -Ukamakonda kwambiri zosangalatsa, umayenera kudziwa kuti mavuto akukusunzumira mochenjera. “Ichi n’changa” chidapinditsa mchira wa nyani. -Nthawi zina chifukwa cha umbombo timawonongetsa zinthu. Munthu angaganize kuti, “Ndikatulutsa pano ndidya ndi anzangawa,” akamati akaone amakapeza zawonongeka. “Ichi n’changa” chinaolera pansalu. -Kuumira kumachititsa kuti zinthu ziwonongeke. “Ichi n’chiyani” n’kulinga muli awiri. -Anthu akakhala awiri amatha kuchita zinthu modalirana ndipo amatha kuthandizana wina akapeza mavuto. “Ichi n’chiyani” n’kulinga muli awiri. -Munthu aliyense amafuna wina woti azimuphunzitsa, 272