Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 272

Miyambi ya Patsokwe Ya M’mitengero “Akuchita dala” adapita ndi madzi. -Tisamalekerere anthu akuchita zoipa kapenanso akusochera pongoganiza kuti adziwa chochita popeza ndi aakulu msinkhu kapena ophunzira kwambiri. Mpofunika kuwachenjeza ndi ku- wathandiza kuti asagwere m’mavuto. “Andilekere” adapha make. -Kuti zinthu zitiyendere bwino, tizipempha mnzeru kwa ena, apo ayi tikhoza kuchita zinthu zomwe tinganong’oneze nazo bondo. “Bongololo ndi ndiwo” uli ndi anzako amene umadya nawo. -Umboni umafunika ngati ukuchita zinthu kuti udziwe ngati ukulondoladi. “Chitachita” sachichitika. -Kuumiriza kapena kuzunza anthu pogwira ntchito sikuthandi- za, chifukwa mapeto ake ntchitoyo ndi imene imawonongeka. “Chitani” adagulira nkhwangwa matowo. -Pafunika kuganizira mofatsa tisanagule chinthu chifukwa mwina tikhoza kungowononga ndalama pachinthu chopanda ntchito kwenikweni. “Chitani” adakafera kunyanja. -Munthu wolamula asodzi anafera kunyanja chifukwa chosadzi- wa kupalasa bwato. Nthawi zonse ankangouza ena kuti apalase. Pofuna kuchita kanthu kena pafunika kufunsa ena kuti atithan- dize kachitidwe kake, kenaka n’kuganizira bwino ngati tingathe. Zinthu zoumiriza sizichita bwino. “Diso la Lumbe lili m’kamwa,” n’kulinga utaliona. -Sibwino kumanena zinthu zimene sukuzidziwa bwinobwino. 271