Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 270

Miyambi ya Patsokwe kudzamuona kuti adzamupatse mphatso. Ziliko n’kulinga utatosako. -Si bwino kutsimikizira chinthu usadapeze umboni wokwanira. Umboni weniweni umafunika kuchoka pa zimene waziona. Zimene wamkulu angaone munthu wamkulu atakhala pansi zingapose zimene mwana angaone ataimirira. -Akuluakulu amadziwa zambiri chifukwa akumana ndi zambiri pamoyo wawo. Ndi bwino kumamvera malangizo awo. Zina kambu zina leku. -Umafunika kusankha zoyenera kuyankhula kapena ayi. Zinapangana zinaulukira pamodzi. -Tiyenera kumachita zinthu mogwirizana. Zingale akaipa, aipa ndi nthenga zomwe. -Munthu woipa mtima amaipa ndi mawu komanso zochita zom- we. Zochita zakezo zimakhudzanso abale ake. Zingalume phula nditenga. -Mawuwa amanenedwa kuti ngakhale akumane ndi mavuto otani, sasiya mpaka atapeza chimene akufuna. Zingwinjiri sizipanganika, zimalira m’thumba la mbala. -Munthu wina ataba zingwinjiri anagwidwa zitalira m’thumba. Choipa sichingabisike chimaululika. Zingwinjiri zimalira zikakhala ziwiri. -Kuti zinthu ziyende timafunika kuthandizana. Zingwinjiri zimalira ziwiri, osati chimodzi. -Anthu akakhala awiri amathandizana pa zambiri. Munthu aka- khala wodzikonda zikamuvuta amasowa womuthandiza. Zinthu zimayenda ndi zinzake. -Anthu opeza mofanana amagwirizana. 269