Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 268

Miyambi ya Patsokwe Zakumva zimapweteketsa mutu. -Osamangomvera zilizonse chifukwa zina zimakhala zabodza ndipo zimangokupatsa nkhawa. Zakusimba saulula. -Tizisunga chinsinsi, osamangoulula chilichonse chimene tamva ngati kuti kamwa lathu lili ndi chiboo. Zala sizifanana, nawoso anthu amasiyina. -Tiyenera kumachitira aliyense mofanana. Ngakhale kuti zala ndi zotalika mosiyanasiyana, zonse zimafuna kusamaliridwa mofanana. Zam’dengu zimapindula ukachita khama. -Malonda amafunika khama komanso kulimba mtima. Zamwini sakulira mwendo. -Si bwino kumachita matama chifukwa cha zinthu za eni kapena kumanyoza ena chifukwa cha chuma cha abale athu. Zamwini savalira thewera. -Tisamalowerere nkhani za anthu ena. Zanga zili kuphiri, zifulumira kutsika. -Tisamakongole tilibe podalira. Zangazanga zidathyola bwampini msana. -Munthu amene amangosonkhanitsa zinthu zomwe sangazig- wiritse ntchito ndi wopusa chifukwa amangovutika. Zaona atondo n’zolaula. -Atondo ndi mbewa. Mbewazi zinakumana ndi mavuto aakulu zitakodwa mumsampha. Aliyense akhoza kukumana ndi mavuto. Zathu, salowa m’khola. -Munthu m’modzi sakhala ndi mphamvu pa zinthu zagulu. 267