Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 267

Miyambi ya Patsokwe Za eni n’za eni, madzi amoto satentha nyumba. -Sitiyenera kumajijirikira zinthu za eni chifukwa tikhoza kungopusapo. Za kumzinda saulura. -Ndi bwino kuti tizisunga chinsinsi cha zimene tamva kapena kuona. Zabwino zili m’tsogolo. -Ngati munthu utayesetsa kuchita khama, ukhoza kukhala ndi tsogolo labwino. Zachoka ndundu tiyanike inswa. -Mwambiwu ndi wofanana ndi wakuti, “Achoke malizagudu, ti- yanike inswa ziume.” Umanenedwa posangalala kuti anthu amene sumafuna kuti akhalepo ukamachita zinazake achoka. Zachoka ndundu tiyanikeko inswa. -Anthu ena omwe safuna kuti anzawo amveko zachinsinsi zawo amayesetsa kuti akambirane zachinsinsizo ena aja akachokapo kapena amapita pamalo oduka mphepo. Zadzera usetekera, mkombaphala anaduka chala. -Chala chamkombaphala chikhoza kuduka chifukwa chochig- wiritsa ntchito udyo. Tizichita zinthu moyenera. Zafera m’mazira. -Zalephereka, sizinapite patali. Zakuba sizilemeretsa. -Munthu amene ali ndi zinthu zakuba sazisamalira ngati mmene zikanakhalira akanagwira ntchito. Zakumva zimaondetsa. -Osamangomvera zilizonse chifukwa zina zimakhala zabodza ndipo zimangokupatsa nkhawa. 266