Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 264

Miyambi ya Patsokwe Wotuwa m’pemphe mafuta. -Osauka nthawi zina amatha kukhala ndi zinthu zimene olemera alibe, monga masingano. Wotuwa ndiye amafuna mafuta. -Ndi munthu amene ali pamavuto amene amayesetsa kuti apeze zimene akufuna. Woumba mbiya alibe mkhate. -Si bwino kumaumira kugwiritsa ntchito zomwe tili nazo. Woumba mbiya amaphikira m’phale. -Nthawi zina munthu wogwira ntchito zaluso sakonda kutengako chimodzi chifukwa choganiza kuti akatero akuwo- nonga. Iye amagwiritsa ntchito zipangizo zakutha kapena zosweka. Woumba mbiya saphikira m’phale. -Si bwino kumaumira kugwiritsa ntchito zomwe tili nazo. Woumiriza ndiye amapha nyama. -Nthawi zina chinthu choumirizidwa ndi chimene chimatheka komanso kuchitidwa bwino kwambiri. Wovala nyanda salumpha moto. -Nyanda ndi kampango komwe azimayi amavala m’chiuno. Nyanda sichedwa kugwirira moto. Si bwino kumachita zinthu zimene zingatiike m’mavuto monga kuchita chiwerewere ndi zi- na. Wovinidwa sapisa dzanja m’mphika wa ndiwo. -Tiyenera kusiya kuchita zachibwana tikakula. Woyenda ndi lupanga amafa ndi lupanga lomwelo. -Chinthu chimene umakonda n’chimene chimakupha. 263