Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 263

Miyambi ya Patsokwe Wosoka mphasa amagonera pazidutswa. -Nthawi zina munthu wogwira ntchito zaluso sakonda kutengako chimodzi chifukwa choganiza kuti akatero akuwo- nonga. Iye amagwiritsa ntchito zipangizo zakutha kapena zosweka. Mwachitsanzo, woluka mphasa akhoza kumagona pansi, akasoka mphasa kumangogulitsa. Wosoka mphasa amagona pamachika. -Nthawi zambiri anthu amene amasoka mphasa ndi amene ama- gonera mphasa zakutha. Ndi bwino kumasungako zinthu zina kuti tigwiritse ntchito. Wosuma chakudya alibe mawu. -Ngakhale tikusowa zinthu zina, tiyesetse kumakhutitsidwa ndi zomwe tili nazo. Wotchera ulimbo satsokomora. -Pa mlandu timafunika kuyankhula mosamala kuti tisaulule zi- na. Wotengera Nguluwe kuutsa n’chayamba kale. -Anthu amene amavumbulutsa nguluwe kutchire n’kuigwira amafunika kukhala oti anayamba kale. Ukapeza ena akuchita zinthu zachilendo si bwino kungoyamba kuchita nawo, mwina iwowo amadziwa machitidwe ake. Wothabe upse mbala. -Ukamayenda ndi anthu oipa, usamadabwe ukagwera m’mavuto. Wotsirira anzake amatsiriridwa. -Ukachitira anzako zabwino nawonso amakuchitira zabwino. Wotuwa mpake mafuta. -Tiyenera kuthandiza ena omwe akuvutika. 262