Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 262

Miyambi ya Patsokwe Wopunduka n’Chauta, mpembedzeni. -Tiyenera kulemekeza anthu ngakhale atakhala wolumala chifu- kwa nawonso ndi ana a Mulungu. Wopupuluma anadzikodzera chifukwa cha mvula yongodutsa. -Mawuwa anabwera chifukwa cha munthu wina yemwe ankafu- na kutaya madzi. Ndiye poona kuti mvula ikubwera ndipo anyowabe, anangodzikodzera koma mvulayo inangolambalala umo, osamunyowetsa moti anachita manyazi kwambiri. Tisama- pupulume pochita zinthu. Wopusa amamanga nyumba, wochenjera nagula. -Ndi bwino kumaganiza kaye tisanachite chinthu kuopa kuchita zinthu zopanda mnzeru. Wopusa anaomba ng’oma, wochenjera navina. -Nthawi zina anthu amene amaoneka opusa ndi amene anga- tithandize. Tiziona ena kukhala otiposa pa chinachake. Wosamva adamva nkhwangwa ili m’mutu. -Munthu wosamvera malangizo amadzawamvera atakumana kale ndi mavuto. Kumamva nkhwangwa itafika kale m’mutu komwe ndi kumva mochedwa. Wosamva za anzake n’chitsiru. -Munthu amene samva za anzake amakhala chitsiru, wopulukira komanso wosadziwa kanthu chifukwa saphunzira chilichonse kuchokera kwa ena. Wosamvera za anzake adalira ching’ang’adza. -Munthu amene ndi wosamvera ena, amadzilirira yekha aka- kumana ndi mavuto. Wosauka ndiye wolemera. -Wosauka ndiye amapeza tulo komanso kusangalala ndi zomwe wapeza pomwe wolemera sapeza tulo. 261