Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 260

Miyambi ya Patsokwe wochitanso zina. Wokaona nyanja anakaona ndi mvuu zomwe. -Ukayendera zina umatha kukakumananso ndi zina zomwe sumayembekezera. Wokoma atani wonga fungwe. -Mawuwa amanenedwa munthu akamadandaulira anthu osaya- mika ngakhale utawachitira zabwino. Wokoma sagonera. -Anthu abwino sakhala moyo nthawi yaitali. Wokumba ndi amene amayenda ndi mchopolo. -Mchopolo ndi ndodo yokumbira. Munthu sangakumbe popan- da chokumbira. Tiyenera kukonzekera bwino tisanayambe ku- chita chilichonse. Wokwatira azidya mapira. -Pabanja pamakhala mavuto ambiri omwe amafunika kupirira. Ndiye mapira ndi mbewu imene imapirira chilala. Choncho, kudya mapira kukutanthauza kuti munthu amene ali pabanja ayenera kukhala wopirira. Wolanga mwambo sachita. -Anthu ena amangodziwa kuuza anzawo zochita koma iwowo osachita. Kuti malangizo akhale ogwira mtima umafunika uyambe kaye iweyo kuwatsatira. Wolemera ndi amene amakhutira ndi zomwe ali nazo. -Ngakhale munthu atakhala ndi zochuluka bwanji, koma osama- khutira, munthu woteroyo sangakhale wolemera. Kulemera kwenikweni n’kukhutira ndi zimene uli nazo. Wolira samugwira pakamwa. -Munthu amene akulira mumafunika kumusiya kuti ayankhule zakukhosi kwake. 259