Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 26

Miyambi ya Patsokwe Chalimba chalimba, shati sikhala yopanda kolala. -Ngakhale chinthu chikhale champhamvu, chimasowabe china chochichirikiza. Aliyense ndi wofunika. Chalowa m’khutu chayanza malo. -Chimene munthu wamva sangachitulutsenso. Choncho, mpo- funika kuchenjera polankhula kuopa kulakwitsa. Chalowa m’khutu, chalowa. -Zimene munthu wamva, zimakhala kuti wazimva basi. Sungachitenso chilichonse kuti zibwerere. Tizisamala ti- sanayankhule. Chambo chimaona konse. -Munthu ukakhala pabanja, si bwino kumathandiza abale ako okha. Umayenera kumathandizanso abale a mkazi kapena mwamuna wako. Chamkuka nkhali yagaga. -Mawu amenewa amanena za munthu waulesi, wongokonda kukhala m’nyumba. Chomwe amadziwa ndi kudya basi. Chamuna sayanika. -Munthu ukakhala ndi mphamvu usamadzionetsere, chifukwa tsiku lina umadzakumana ndi anzako omwe amadzakuphu- vumula n’kukuchititsa manyazi. Chamwini m’chamwini, ungalimbe maka. -Anthu ena maso amangokhala pa zinthu za anzawo, osakhutitsidwa ndi zomwe ali nazo. Tifunika kumachenjera ndi anthu amenewa. Osamadalira kwambiri zinthu za ena. Changodza m’chironda, mankhwala palibe. -Mawuwa amanenedwa munthu akamadandaula kuti, ngakhale mavuto monga matenda komanso milandu abwera, palibe njira yowathetsera. 25