Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 258

Miyambi ya Patsokwe Watuluka m’mphuno n’kulowa m’kamwa. -Mawuwa amanena za munthu amene sanakwatire kutali, mwina wakwatira pafupi ndi mudzi wake, kapena wakwatira msuweni wake. Wavina kumadzi. -Mawuwa amanena mokokomeza za munthu amene amatamba usiku. Kumadzi ndi kumtsinje. Malinga ndi zikhalidwe za ku Africa kuno, ena amakhulupirira za ufiti ngakhale palibe umbo- ni wokwanira woti ulipodi. Wawona Nkhanga maanga wataya Nkhwali. -Si bwino kutengeka ndi zinthu chifukwa cha maonekedwe. Ukhoza kupezeka kuti wataya mwayi wopezapeza. Wayanja mbatata, wataya mpeni. -Mawuwa amatanthauza kusiya zinthu zenizeni n’kumalimbana ndi zinthu zosafunika. Wayenda wapenga, wagona wafa. -Ngati munthu wapita kuchilendo ayenera kumakumbukira kuti tsiku lina adzabwerera kwawo. Wochenjera ndi munthu amene amati akaona tsoka amabisala, koma chitsiru chimangopitabe n’kukumana ndi mavuto. -Mwambiwu ndi wochokera m’Baibulo koma anthu ambiri amaugwiritsa ntchito pochenjeza anthu ena omwe amachitabe zinthu zomwe akudziwa kuti zikhoza kuwaika m’mavuto. Wodya nyemba amaiwala, koma wotaya makoko saiwala. -Zimene anthu ena amachita amaziiwala, koma amene wachitiridwayo zimavuta kuti aziiwale. Wodya za kuchinamwali akudza ndi tambala. -Mawuwa amatanthauza kuti munthu amene amakadya 257