Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 255

Miyambi ya Patsokwe Wanga ndi wamalonda. -Munthu woumira safuna kungopereka zinthu mwaulere. Wangoopa njokaluzi. -Kumeneku ndi kuopa chinthu chosayenera kuopedwa. Wani tambala ilibe chenje. -Pabanja pamafunika kukhala mwamuna mmodzi ndi mkazi mmodzi basi. Wanjala safuna ndiwo. -Munthu amene wayamba kuona kuti ndiwo zake sizikukoma amakhala kuti wakhuta. Wanjala saona zonsezo amangoti bola akhute. Wanjala salima, amalima ngwokhuta. -Kuti munthu agwire ntchito amafunika kudyera kaye. Wanjiru sagonera, mvula yake ndi imodzi. -Anthu oipa sakhalitsa. Wanyanga aferanji? -Mwambiwu umatanthauza kuti n’chifukwa chiyani munthu wodalira mankhwala amafa? Aliyense adzafabe afune asafune. Waona kamwana tola, ukulu n’kuona kako. -Munthu akayenda ndi mwana amayenera kukhala wokonze- kera. Si bwino kumangodalira mwanayo pa chilichonse. Waona mawanga a Nkhanga wataya Nkhwali. -Ukamamvera za anthu umatha kutaya mwayi womwe uli nawo kale. Ukakhala ndi chinthu si bwino kuchinyoza chifukwa waona china chokongola kwambiri kuopera kuti ungataye chabwino n’kulephera kupeza chinacho. Wapala moto kudambwe eni ake alipo. -Mawuwa amatanthauza kuti wapalamula. Kapena kuyankhula 254