Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 254
Miyambi ya Patsokwe
Wamtengatenga sagona.
-Munthu akafuna kuchita chinthu amafunika kuchita khama
m’malo mochita ulesi. Ngati anthu amene amanyamula zinthu
samatopa kapena kugona.
Wamuonetsa chidameta mduliro nyani.
-Mawuwa amatanthauza kukhaulitsa munthu wina.
Wamuonetsa chidameta nkhanga mpala
-Mawuwa amatanthauza kukhaulitsa munthu wina.
Wamusiya ali njo! pabwalo.
-Mawuwa amanenedwa anthu akamaseka munthu yemwe pab-
walo lamilandu amasowa chonena. Amayamba kumukuwiza
n’kumauza amene akuoneka kuti tikuwayenderawo mawu ame-
newa.
Wamva m’mimba ndi amene amatsegula chitseko.
-Munthu amene ali pamavuto ndi amene amachitapo kanthu
kuti mavutowo amuchoke.
Wandalama sayimba nthungululu.
-Si bwino kumanyada ukakhala pabwino.
Wandibisira mpeni kumphasa.
-Mawuwa amanenedwa ngati munthu akudandaula kuti wina
wawachitira chiwembu.
Wandigwiritsa fuwa lamoto.
-Mawuwa amanenedwa ndi munthu amene wapusitsidwa ndi
winawake.
Wandiviika m’mbuna.
-Mawuwa amatanthauza kusungira munthu chakukhosi kuti
udzamubwezere nayenso akadzalakwa.
253