Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 253

Miyambi ya Patsokwe bwino. Si bwino kutengeka ndi zinthu chifukwa cha maon- ekedwe. Ukhoza kupezeka kuti wataya mwayi wopezapeza. Walira mvula walira matope. -Chilichonse chili ndi zovuta zake, choncho si bwino kungosiya kuchita zinthuzo chifukwa choti ukukumana ndi mavuto. Tiyenera kumavomereza zotsatira za zomwe tasankha monga kulowa m’banja. Wamenya chikambakamba mtima uli pansi. -Mawuwa amatanthauza kuti munthu walephera kuchita zimene umafunadi kuchita. Wamisala anaona nkhondo. -Si bwino kunyoza munthu chifukwa santha kuchita zinthu zina chifukwa ali ndi mbali ina yomwe amachita bwino. Osamanyoza zonena za ena ngakhale kuti ndi ana kapena osaphunzira. Chifu- kwa nthawi zina zimene anganene zimakhala zothandiza kwam- biri. Wam’kachisi amadya zam’kachisi. -Munthu amapeza zimene akufunikira pamene amagwira ntchi- to. Wamkulu salakwa. -Munthu wamkulu ngakhale alakwitse sauzidwira pagulu pom- wepo kuti walakwa, koma kumukokera pambali. Wampota bwanji khobwe ndili ku ula? -Mkazi anapota khobwe kapena kuti kumupanga chipere, pom- we mwamuna wake ankakonda wochita kubwira. Zimenezi zi- nakhumudwitsa mwamunayo moti anakwiya. Chilichonse chimakhala ndi dongosolo lake, choncho ndi bwino kumafunsa tisanachite zinthu. 252