Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 251

Miyambi ya Patsokwe n’kupita kwa wogulitsa n’kukapeza zitatha. Wogulitsayo an- gamuuze kuti, “waimba yakale, ana aakazi abwerera.” Waisenzera pankhongo. -Amenewa ndi mawu okokomeza onena kuti nkhani sanaimvet- se munthuyo. Wakaduka alibe anansi. -Munthu ukakhala wakaduka anthu amakuthawa. Wakalamba Wafuna. -Masiku ano anthu ambiri akumachita zinthu zomwe zingathan- dize kuti asaoneke okalamba kwambiri, ndiye akamatchula mwachining’a amangoti, “wakalamba wafuna.” Wakhala kuutsi dala. -Munthu akamafuna kuchoka amachita zinazake kuti achokepo. Mwambiwu umaziyerekezera ndi kukhala dala kuutsi kuti uziti wachoka chifukwa utsi ukukupwetseketsa maso. Wakhalira khute. -Mawuwa amatanthauza kudikirira zinthu zimene sitingazipeze. Wakhate samunamiza nsapato. -Tisamalonjeze zinthu zomwe sitingakwanitse kuchita, monga kunamiza wakhate kuti umugulira nsapato. Komanso si bwino kulonjeza munthu mphatso yomwe sangathe kuigwiritsa ntchi- to. Umenewu umakhala mwano. Wakhungu akakuuza kuti ndikugenda, samala, waponda mwala! -Munthu amene sumaganizira akakuuza zinazake zachilendo, dziwa kuti palipo pamene akudalira. Wakhungu akati ndikugenda, ndiye kuti waponda mwala. -Munthu akamachita chinachake amakhala ndi podalira. 250