Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Miyambi ya Patsokwe | Page 25

Miyambi ya Patsokwe yangogwa. Komanso munthu amene wamwalira sangachite chilichonse, ngati akuyankhula ndiye kuti adakali moyo. Chakumbakumba chalema, chatenga mchira chayesa mala. -Nthawi zina munthu amasiya kuyesayesa kuthetsa mavuto n’kuyamba kumangokhala poganiza kuti atha okha. Chakuti “tswo” chakuyambira, chakuti “tseche” chakupha. -Tisamadandaule ndi zovuta zomwe zimabwera pang’onopang’ono koma zomwe zimabwera kamodzim’ka- modzi. Chakwathu n’chakwathu adamangira nkhokwe m’nyumba. -Ndi bwino kumamvera zimene ena akunena. Osamangoumirira njira zakale popanda chifukwa chomveka bwino, chifukwa mapeto ake timapezeka kuti talakwitsa. Chala chimodzi sichiswa nsabwe. -Palibe munthu amene angathe kuchita zonse payekha. Chon- cho, ndi bwino kumadalirana. Pogwira ntchito kapena pothetsa vuto, thandizo la anthu ena ndi lofunika. Chala sicholoza mwini. -Munthu sakonda kuona kulakwa kwake koma kwa ena. Chalaka (chakanika) Bakha, Nkhuku singatole. -Chimene chakanika katswiri munthu wamba sangachithe. Chalaka Galu, fupa la matongwe. -Mawu amenewa amanena za munthu yemwe ndi wosamva ngakhale mutamulangiza motani. Amakhala ngati fupa louma lomwe agalu alephera kuliswa. Chalaka Nyani chili ndi khambi. -Munthu akasiya chizolowezi chake ndiye kuti chilipo chimene chamudabwitsa kapena chamuchititsa mantha. 24